Masalmo 133

Cikondano ca abale ndi cokoma

Nyimbo yokwerera; ya Davide.

1 Onani, nkokoma ndi kokondweretsa ndithu

Kuti abale akhale pamodzi!

2 Ndiko ngati mafuta a mtengo wace pamutu,

Akutsikira ku ndebvu,

Inde ku ndebvu za Aroni;

Akutsikira ku mkawo wa zobvala zace

3 Ngati mame a ku Hermoni,

Akutsikira pa mapiri a Ziyoni:

Pakuti pamenepo Yehova analamulira dalitsolo,

Ndilo moyo womka muyaya,