Masalmo 129

Israyeli asautsidwa koma osafafanizidwa

Nyimbo yokwerera.

1 Anandisautsa kawiri kawiri kuyambira ubwana wanga,

Anene tsono Israyeli;

2 Anandisautsa kawiri kawiri kuyambira ubwana wanga;

Koma sanandilaka.

3 Olima analima pamsana panga;

Anatalikitsa mipere yao.

4 Yehova ndiye wolungama;

Anadulatu zingwe za oipa.

5 Acite manyazi nabwerere m’mbuyo.

Onse akudana naye Ziyoni.

6 Akhale ngati udzu womera patsindwi,

Wakufota asanauzule;

7 Umene womweta sadzaza nao dzanja lace,

Kapena womanga mitolo sakupatira manja.

8 Angakhale opitirirapo sanena,

Dalitso la Mulungu likhale pa inu;

Tikudalitsani m’dzina la Yehova.