Okhulupirira Yehova akhazikika mtima
Nyimbo yokwerera.
1 Iwo akukhulupirira Yehova
Akunga phiri la Ziyoni, losasunthika, likhazikika kosatha,
2 Monga mapiri azinga Yerusalemu,
Momwemo Yehova azinga anthu ace,
Kuyambira tsopano kufikira nthawi zonse.
3 Pakuti ndodo yacifumu ya coipa siidzapumula pa gawo la olungama;
Kuti olungama asaturutse dzanja lao kucita cosalungama,
4 Citirani cokoma, Yehova, iwo okhala okoma;
Iwo okhala oongoka mumtima mwao.
5 Koma iwo akupatuka kutsata njira zao zokhotakhota,
Yehova adzawacotsa pamodzi ndi ocita zopanda pace.
Mtendere ukhale pa Israyeli.