Mulungu Msungi wokhulupirika wa anthu ace
Nyimbo yokwerera.
1 Ndikweza maso anga kumapiri:
Thandizo langa lidzera kuti?
2 Thandizo langa lidzera kwa Yehova,
Wakulenga zakumwamba ndi dziko lapansi.
3 Sadzalola phazi lako literereke:
Iye amene akusunga sadzaodzera.
4 Taonani, wakusunga Israyea
Sadzaodzera kapena kugona.
5 Yehova ndiye wakukusunga;
Yehova ndiye mthunzi wako wa ku dzanja lako lamanja.
6 Dzuwa silidzawamba usana,
Mwezi sudzakupanda usiku.
7 Yehova adzakusunga kukucotsera zoipa ziri zonse;
Adzasunga moyo wako.
8 Yehova adzasungira kuturuka kwako ndi kulowa kwako,
Kuyambira tsopano kufikira nthawi zonse.