Masalmo 115

Mulungu ndi wa ulemerero, mafano ndiwo acale

1 Kwa ife ai, Yehova, kwa ife ai, Koma kwa dzina lanu patsani ulemerero,

Cifukwa ca cifundo canu, ndi coonadi canu.

2 Aneneranji amitundu,

Ali kuti Mulungu wao?

3 Koma Mulungu wathu ndiye ali m’mwamba;

Acita ciri conse cimkonda.

4 Mafano ao ndiwo a siliva ndi golidi,

Nchito za manja a anthu.

5 Pakamwa ali napo, koma osalankhula;

Maso ali nao, koma osapenya;

6 Makutu ali nao, koma osamva;

Mphuno ali nazo, koma osanunkhiza;

7 Manja ali nao, koma osagwira;

Mapazi ali nao, koma osayenda;

Kapena sanena pammero pao,

8 Adzafanana nao iwo akuwapanga;

Ndi onse akuwakhulupirira,

9 Israyeli, khulupirira Yehova:

Ndiye mthandizi wao ndi cikopa cao.

10 Nyumba ya Aroni, khulupirira Yehova:

Ndiye mthandizi wao, ndi cikopa cao.

11 Inu akuopa Yehova, khulupirirani Yehova;

Ndiye mthandizi wao ndi cikopa cao.

12 Yehova watikumbukila; adzatidalitsa:

Adzadalitsa nyumba ya Israyeli;

Adzadalitsa nyumba ya Aroni.

13 Adzadalitsa iwo akuopa Yehova,

Ang’ono ndi akuru.

14 Yehova akuonjezereni dalitso, Inu ndi ana anu.

15 Odalitsika inu a kwa Yehova,

Wakulenga kumwamba ndi dziko lapansi.

16 Kunena za kumwamba, kumwamba ndiko kwa Yehova;

Koma dziko lapansi analipereka kwa ana a anthu.

17 Akufa salemekeza Yehova,

Kapena ali yense wakutsikira kuli cete:

18 Koma ife tidzalemekeza Yehova

Kuyambira tsopano kufikira nthawi yonse.

Haleluya.