Masalmo 114

Alemekeze Mulungu pa cipulumutso cija ca m’Aigupto

1 M’mene Israyeli anaturuka ku Aigupto,

Nyumba ya Yakobo kwa anthu a cinenedwe cacilendo;

2 Yuda anakhala malo ace oyera, Israyeli ufumu wace.

3 Nyanjayo inaona, nithawa;

Yordano anabwerera m’mbuyo.

4 Mapiri anatumphatumpha ngati nkhosa zamphongo,

Timapiri ngati ana a nkhosa.

5 Unathawanji nawe, nyanja iwe?

Unabwerereranji m’mbuyo, Yordano iwe?

6 Munatumpha-tumphiranji ngati nkhosa zamphongo, mapiri inu?

Ngati ana a nkhosa, zitunda inu?

7 Unjenjemere, dziko lapansi iwe, pamaso pa Ambuye,

Pamaso pa Mulungu wa Yakobo;

8 Amene anasanduliza thanthwe likhale thawale lamadzi,

Nsangalabwi ikhale kasupe wamadzi.