Masalmo 113

Anthu onse alemekeze dzina la Mulungu wothandiza aumphawi

1 Haleluya;

Lemekezani, inu atumiki a Yehova;

Lemekezani dzina la Yehova,

2 Lodala dzina la Yehova.

Kuyambira tsopano kufikira kosatha.

3 Citurukire dzuwa kufikira kulowa kwace

Lilemekezedwe dzina la Yehova.

4 Yehova akwezeka pamwamba pa amitundu onse,

Ulemerero wace pamwambamwamba.

5 Akunga Yehova Mulungu wathu ndani?

Amene akhala pamwamba patali,

6 Nadzicepetsa apenye

Zam’mwamba ndi za pa dziko lapansi.

7 Amene autsa wosauka lrumcotsa kupfumbi,

Nakweza waumphawi kumcotsa kudzala.

8 Kuti amkhalitse pamodzi ndi akulu,

Pamodzi ndi akulu a anthu ace.

9 Asungitsa nyumba mkazi wosaonamwana,

Akhale mai wokondwera ndi ana.

Haleluya.