Masalmo 110

Ufumu wa Ambuye

Salmo la Davide,

1 Yehova ananena kwa Ambuye wanga, Khalani pa dzanja lamanja langa,

Kufikira nditaika adani anu copondapo mapazi anu.

2 Yehova adzatumiza ndodo ya mphamvu yanu kucokera ku Ziyoni;

Citani ufumu pakati pa adani anu.

3 Anthu anu adzadzipereka eni ace tsiku la camuna canu:

M’moyera mokometsetsa, mobadwira tnatanda kuca,

Muli nae mame a ubwana wanu.

4 Yehova walamulira, ndipo sadzasintha,

Inu ndinu wansembe kosatha

Monga mwa cilongosoko ca Melikizedeke.

5 Yehova pa dzanja lamanja lako

Adzaphwanya mafumu tsiku la mkwiyo wace.

6 Adzaweruza mwa amitundu,

Adzadzaza dziko ndi mitembo;

Adzaphwanya mitu m’maiko ambiri.

7 Adzamwa ku mtsinje wa panjira;

Cifukwa cace adzaweramutsa mutu wace.