Masalmo 11

Yehova asunga anthu ace nalanga oipa

Kwa Mkulu wa Nyimbo: Salmo la Davide.

1 Ndakhulupirira Yehova:

Mutani nkunena kwa moyo wanga,

Thawirani ku phiri lanu ngati mbalame?

2 Pakuti, onani, oipa akoka uta,

Apiringidza mubvi wao pansinga,

Kuwaponyera mumdima oongoka mtima.

3 Akapasuka maziko,

Wolungama angacitenji?

4 Yehova ali m’Kacisi wace woyera,

Yehova, mpando wacifumu wace uli m’Mwamba;

Apenyerera ndi maso ace, ayesa ana a anthu ndi zikope zace.

5 Yehova ayesa wolungama mtima:

Koma moyo wace umuda woipa ndi iye wakukonda ciwawa.

6 Adzagwetsa pwata pwata misampha pa oipa;

Moto ndi miyala yasuifure, ndi mphepo yoopsa zidzawagawikira m’cikho cao.

7 Pakuti Yehova ndiye wolungama; akonda zolungama:

Woongoka mtima adzapenya nkhope yace.