Davide ayimbira Mulungu womgonjetsera adani
Nyimbo. Salmo la Davide.
1 Wakhazikika mtima wanga, Mulungu;
Ndidzayimba, inde ndidzayimba zolemekeza, ndiko ulemerero wanga.
2 Galamukani, cisakasa ndi zeze;
Ndidzauka ndekha mamawa.
3 Ndidzakuyamikani mwa mitundu ya anthu, Yehova:
Ndipo ndidzayimba zakukulemekezani mwa anthu.
4 Pakuti cifundo canu ncacikuru kupitirira kumwamba,
Ndi coonadi canu kufikira mitambo.
5 Kwezekani pamwamba pa thambo, Mulungu;
Ndi ulemerero wanu pamwamba pa dziko lonse lapansi.
6 Kuti okondedwa anu alanditsidwe,
Pulumutsani ndi dzanja lanu lamanja ndipo mutibvomereze.
7 Mulungu analankhula m’ciyero cace; ndidzakondwerera:
Ndidzagawa Sekemu; ndidzayesa muyeso cigwa ca Sukoti.
8 Gileadi ndi wanga: Manase ndi wanga;
Ndi Efraimu ndiye mphamvu ya mutu wanga;
Yuda ndiye wolamulira wanga.
9 Moabu ndiye mkhate wanga;
Pa Edomu ndidzaponya nsapato yanga;
Ndidzapfuulira Filistiya,
10 Adzandifikitsa ndani m’mudzi wa m’linga?
Adzanditsogolera ndani ku Edomu?
11 Si ndinu Mulungu, amene mwatitaya
Osaturuka nao magulu athu?
12 Tithandizeni mumsauko;
Pakuti cipulumutso ca munthu ndi cabe.
13 Mwa Mulungu tidzacita molimbika mtima:
Ndipo Iye adzapondereza otisautsa.