Masalmo 101

Davide akuti adzasamala okhulupirika nadzacotsa oipa

Salmo la Davide.

1 Ndidzayimba za cifundo ndi ciweruzo;

Ndidzayimba zakukulemekezani Inu, Yehova.

2 Ndidzacita mwanzeru m’njira yangwiro;

Mudzandidzera liti?

Ndidzayenda m’nyumba mwanu ndi mtima wangwiro.

3 Sindidzaika cinthu coipa pamaso panga;

Cocita iwo akupatuka padera cindiipira;

Sicidzandimamatira.

4 Mtima wopulukira udzandicokera;

Sindidzadziwana naye woipa.

5 Wakuneneza mnzace m’tseri ndidzamdula;

Wa maso odzikuza ndi mtima wodzitama sindidzamlola.

6 Maso anga ayang’ana okhulupirika m’dziko, kuti akhale ndi Ine;

Iye amene ayenda m’njira yangwiro, iyeyu adzanditumikira Ine.

7 Wakucita cinyengo sadzakhala m’kati mwa nyumba yanga;

Wakunena mabodza sadzakhazikika pamaso panga.

8 Mamawa onse ndidzadula oipa onse a m’dziko;

Kuduliratu onse akucita zopanda pace ku mudzi wa Yehova.