Masalmo 10

Athamangira Mulungu pothawa adani omtsata

1 Muimiranji patari, Yehova?

Mubisaliranji m’nyengo za nsautso?

2 Podzikuza woipa apsereza waumphawi;

Agwe m’ciwembu anapanganaco.

3 Pakuti woipa adzitamira cifuniro ca moyo wace,

Adalitsa wosirira, koma anyoza Yehova.

4 Woipa, monga mwa kudzikuza kwa nkhope yace, akuti, Sadzafunsira.

Malingaliro ace onse akuti, Palibe Mulungu.

5 Mayendedwe ace alimbika nthawi zonse;

Maweruzo anu ali pamwamba posaona iye;

Adani ace onse awanyodola.

6 Ati mumtima mwace, Sindidzagwedezeka ine;

Ku mibadwo mibadwo osagwa m’tsoka ine.

7 M’kamwa mwace mwadzala kutemberera ndi manyengo ndi kucenjerera;

Pansi pa lilime lace pali cibvutitso copanda pace.

8 Akhala m’molalira midzi;

Mobisalamo akupha munthu wosacimwa:

Ambisira waumphawi nkhope yace,

9 Alalira monga mkango m’ngaka mwace;

Alalira kugwira wozunzika:

Agwira wozunzika, pakumkola m’ukonde mwace.

10 Aunthama, nawerama,

Ndipo aumphawi agwa m’zala zace.

11 Anena m’mtima mwace, Mulungu waiwala;

Wabisa nkhope yace; sapenya nthawi zonse,

12 Ukani, Yehova; samulani dzanja lanu, Mulungu;

Musaiwale ozunzika.

13 Woipa anyozeranii Mulungu,

Anena m’mtima mwace, Simudzafunsira?

14 Mwapenya; pakuti mumayang’anira cibvutitso ndi cisoni kuti acipereke m’manja mwanu;

Waumphawi adzipereka kwa Inu;

Wamasiye mumakhala mthandizi wace.

15 Thyolani mkono wa woipa;

Ndipo wocimwa, mutsate coipa cace kufikira simucipezanso cina.

16 Yehova ndiye Mfumu ku nthawi yamuyaya;

Aonongeka amitundu m’dziko lace.

17 Yehova, mwamva cikhumbo ca ozunzika:

Mudzakhazikitsa mtima wao, mudzachereza khutu lanu:

18 Kuti muweruze mlandu wa amasiye ndi wokhalira mphanthi,

Kuti munthu wa pa dziko lapansi angaonjeze kuopsa.