Masalmo 1

Kusiyana pakati pa olungama ndi oipa

1 WODALA munthuyo wosayenda mu uphungu wa oipa,

Kapena wosaimirira m’njira ya ocimwa,

Kapena wosakhala pansi pa bwalo la onyoza.

2 Komatu m’cilamulo ca Yehova muli cikondwerero cace;

Ndipo m’cilamulo cace amalingima usana ndi usiku.

3 Ndiye akunga mtengo wooka pa mitsinje ya madzi;

Wakupatsa cipatso cace pa nyengo yace,

Tsamba lace lomwe losafota;

Ndipo zonse azicita apindula nazo.

4 Oipa satero ai;

Koma akunga mungu wouluka ndi mphepo.

5 Cifukwa cace oipa sadzaimirira pa mlanduwo,

Kapena ocimwa mu msonkhano wa olungama.

6 Pakuti Yehova adziwa mayendedwe a olungama;

Koma mayendedwe a oipa adzatayika.